31 Ndipo a pfuko la Manase logawika pakati zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ochulidwa maina ao kuti adzalonge Davide mfumu.
32 Ndi a ana a Isakara, anthu akuzindikira nyengo, akudziwa zoyenera Israyeli kuzicita, akuru ao ndiwo mazana awiri; ndi abale ao onse anapenyerera pakamwa pao.
33 A Zebuloni akuturuka kukhamu, opangira nkhondo, monga mwa zida ziri zonse za nkhondo, zikwi makumi asanu, akusunga malongosoledwe a nkhondo ndi mtima wosatekeseka.
34 Ndi a Nafitali atsogoleri cikwi cimodzi, ndi pamodzi nao ogwira zikopa ndi mikondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri.
35 Ndi a Adani akupangira nkhondo zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu ndi limodzi.
36 Ndi a Aseri akuturuka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.
37 Ndi tsidya lga la Yordano a Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la: Manase logawika pakati, ndi zida: ziri zonse za khamu kucita nazo nkhondo, zikwi zana limodzi ndi makumi awiri.