17 Ndipo Paulo anadziitanira kenturiyo wina, nati, Pita naye mnyamata uyu kwa kapitao wamkuru; pakuti ali nako kanthu kakumfotokozera iye.
18 Pamenepo ndipo anamtenga, napita naye kwa kapitao wamkuru, nati, Wam'nsingayo Paulo anandiitana, nandipempha ndidze naye mnyamata uyu kwa inu, ali nako kanthu kakulankhula ndi inu.
19 Ndipo kapitao wamkuru anamgwira dzanja, napita naye padera, namfunsa m'tseri, Ciani ici uli naco kundifotokozera?
20 Ndipo anati, Ayuda anapangana kuti akufunseni mutsike naye Paulo mawa ku bwalo la mirandu, monga ngati mufuna kufunsitsa za iye.
21 Pamenepo musakopedwe nao; pakuti amlalira iye oposa makumi anai a iwo amene anadzitemberera okha kud sadzadya kapena kumwa kufikira atamupha iye; ndipo akonzekeratu tsopano nayang'anira lonjezano lanu.
22 Pamenepo ndipo kapitao wamkuru anauza mnyamatayo apite, namlamulira kuti, Usauze munthu yense kuti wandizindikiritsa izi.
23 Ndipo anaitana akenturiyo awiri, nati, Mukonzeretu asilikari mazana awiri, apite kufikira Kaisareya, ndi apakavalo makumi asanu ndi awiri, ndi anthungo mazana awiri, acoke ora lacitatu la usiku;