12 Ndi pambuyo pace Eleazara mwana wa Dodo M-ahohi, ndiye mmodzi wa atatu aja amphamvu.
13 Anali pamodzi ndi Da vide ku Pasidamimu muja; Afilisti anasonkhanako kunkhondo kumene kunali munda wodzala ndi barele; ndipo anthu anathawa pamaso pa Afilisti.
14 Koma anadziimika pakati pa munda, naulanditsa, nakantha Afilisti; m'mwemo anawapulumutsa Yehova ndi cipulumutso cacikuru.
15 Ndipo atatu a akuru makumi atatu anatsikira kuthanthwe kwa Davide, ku phanga la Adulamu; ndi nkhondo ya Afilisti idamanga misasa m'cigwa ca Refaimu.
16 Pamenepo Davide anali m'linga, ndi boma la askari linali ku Betelehemu.
17 Ndipo Davide analakalaka, nati, Ha! mwenzi wina atandimwetsa madzi a m'citsime ca ku Betelehemu ciri kucipata,
18 Napyola atatuwo misasa ya Afilish natunga madzi ku citsime ca ku Betelehemu ciri kucipata, nabwera nao kwa Davide; koma Davide anakana kumwako, koma anawathirira kwa Yehova;