14 Ndipo anauka nacotsa maguwa a nsembe okhala m'Yerusalemu, nacotsa pofukizira zonunkhira, naziponya m'mtsinje wa Kedroni.
15 Pamenepo anaphera Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi waciwiri, ndipo ansembe ndi Alevi anacita manyazi, nadzipatula, nabwera nazo nsembe zopsereza ku nyumba ya Yehova.
16 Naima m'malo mwao mwa kulongosoka kwao, monga mwa cilamulo ca Mose munthu wa Mulunguyo; ansembe anawaza mwazi, ataulandira ku dzanja la Alevi.
17 Pakuti munali ambiri mumsonkhano sanadzipatula; potero Alevi anayang'anira kupha za Paskha kwa ali yense wosakhala woyera, kuwapatulira Yehova.
18 Pakuti, anthu aunyinji, ndiwo ambiri a Efraimu, ndi Manase, Isakara, ndi Zebuloni, sanadziyeretsa, koma anadya Paskha mosati monga munalembedwa.
19 Koma Hezekiya anawapempherera, ndi kuti, Yehova wabwino akhululukire yense wakuika mtima wace kufuna Mulungu Yehova, Mulungu wa makolo ace, cinkana sanayeretsedwa monga mwa mayeretsedwe a malo opatulika.
20 Ndipo Yehova anamvera Hezekiya, nawaciritsa anthu.