1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Lankhula ndi anthu a Israyeli kuti abwerere m'mbuyo nagone patsogolo pa Pihahiroti, pakati pa Migidoli ndi nyanja yamcere, patsogolo pa Baala-Zefoni; pandunji pace mugone panyanja.
3 Ndipo Farao adzanena za ana a Israyeli, Azimidwa dziko, cipululu cawatsekera.
4 Ndipo ndidzalimbitsa mtima wace wa Farao kuti awalondole; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao ndi pa nkhondo yace yonse; pamenepo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, Ndipo anacita comweco.
5 Ndipo anauza mfumu ya Aigupto kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ace inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ici nciani tacita, kuti talola Israyeli amuke osatigwiriranso nchito?