22 Ansembenso, akuyandikiza kwa Yehova adzipatulitse, angawapasule Yehova.
23 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Anthu sangathe kukwera m'phiri la Sinai; pakuti Inu mwaticenjeza, ndi kuti, Lemba malire m'phirimo, ndi kulipatula.
24 Ndipo Yehova anati kwa iye, Muka, tsika: nukwere iwe ndi Aroni pamodzi ndi iwe; koma ansembe ndi anthu asapyole kukwera kwa Yehova, angawapasule.
25 Pamenepo Mose anawatsikira anthu, nanena nao.