18 Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.
19 Ali yense agona ndi coweta aphedwe ndithu.
20 Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.
21 Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.
22 Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.
23 Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;
24 ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.