28 Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkuru wa anthu a mtundu wako.
29 Usacedwa kuperekako zipatso zako zocuruka, ndi zothira zako. Woyamba wa ana ako amuna undipatse Ine.
30 Uzitero nazo ng'ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wace; tsiku lacisanu ndi citatu uzimpereka kwa Ine.
31 Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; cifukwa cace musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agaru.