4 ndi lamadzi, ndi: lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;
5 ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;
6 mafuta akuunikira, zonunkhira za mafuta odzoza, ndi za cofukiza ca pfungo lokoma;
7 miyala yaberulo, ndi miyala yoika paefodi, ndi pacapacifuwa.
8 Ndipo andimangire malo opatulika; kuti ndikhale pakati pao,
9 Monga mwa zonse Ine ndirikuonetsa iwe, cifaniziro ca kacisi, ndi cifaniziro ca zipangizo zace zonse, momwemo ucimange.
10 Ndipo azipanga likasa la mtengo wasitimu: utali wace mikono iwiri ndi hafu, kupingasa kwace mkono ndi hafu, msinkhu wace mkono ndi hafu.