16 Cikhale campwamphwa, copindika, utali wace cikhato cimodzi, ndi kupingasa kwace cikhato cimodzi.
17 Ndipo uikepo miyala yoikikapo, mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba;
18 ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahaloni;
19 ndi mizere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama;
20 ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; zikhale zogwirika ndi golidi m'zoikamo zao.
21 Ndi miyalayi ikhale monga mwa maina a ana a Israyeli, khumindiawiri, monga maina ao; monga malocedwe a cosindikizira, yonse ikhale monga maina ao, kwa mafuko khumi ndi awiri.
22 Upangenso maunyolo pa capacifuwa ngati zingwe, nchito yopota, ya golidi woona.