3 Ndipo Mose anati, Ndipatuketu, ndikaone cooneka cacikuruco, citsambaco sicinyeka bwanji,
4 Pamene Yehova anaona kuti adapatuka kukapenya, Mulungu ali m'kati mwa citsamba, anamuitana, nati, Mose, Mose. Ndipo anati, Ndiri pano.
5 Ndipo iye anati, Usayandikire kuno; bvula nsapato zako ku mapazi ako, pakuti pamalo pamene upondapo iwe, mpopatulika.
6 Ananenanso Ine ndine Mulungu wa atate wako, Molungu wa Abrahamu, Molungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo. Ndipo Mose anabisa nkhope yace; popeza anaopa kuyang'ana Mulungu,
7 Ndipo Yehova anati, Ndapenyetsetsa mazunzo a anthu anga ali m'Aigupto, ndamvanso kulira kwao cifukwa ca akuwafulumiza; pakuti ndidziwa zowawitsa zao;
8 ndipo ndatsikira kuwalanditsa m'manja a anthu a Aigupto, ndi kuwatumtsa m'dziko lila akwere nalowe m'dziko labwino ndi lalikuru, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi; ku malo a Akanani, ndi Ahiti ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi.
9 Ndipo tsopano, taona kulira kwa ana a Israyeli kwandifikira; ndapenyanso kupsinjika kumene Aaigupto awapsinja nako.