5 ndi kuzokota miyala yoikika, ndi kuzokota mtengo, kucita nchito ziri zonse.
6 Ndipo Ine, taona, ndampatsa Aholiabu, mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani, akhale naye; ndipo ndaika luso m'mitima ya onse a mtima waluso, kuti apange zonse ndakuuza iwe;
7 cihema cokomanako, likasa la mboni, ndi cotetezerapo ciri pamwamba pace, ndi zipangizo zonse za cihemaco;
8 ndi gomelo ndi zipangizo zace, ndi coikapo nyali coona ndi zipangizo zace, ndi guwa la nsembe lofukizapo;
9 ndi guwa la nsembe yopsereza ndi zipangizo zace zonse, ndi mkhate ndi tsinde lace;
10 ndi zobvala zotumikira nazo, ndi zobvala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, zakucita nazo nchito ya nsembe;
11 ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca zonunkhira zokoma za malo opatulika; azicita monga mwa zonse ndakuuza iwe.