9 ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.
10 Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;
11 kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;
12 likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;
13 gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;
14 ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;
15 ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;