16 Ndipo maina a ana amuna a Levi, mwa kubadwa kwao ndiwo: Gerisoni, ndi Kohati, ndi Merari; ndipo zaka za moyo wa Levi ndizo zana limodzi mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri.
17 Ana amuna a Gerisoni ndiwo: Libni ndi Simei, mwa mabanja ao.
18 Ndi ana amuna a Kohati ndiwo: Amramu ndi Izara, ndi Hebroni, ndi Uziyeli; ndipo zaka za moyo wa Kohati ndizo zana limodzi ndi makumi atatu kudza zitatu.
19 Ndipo ana amuna a Merai ndiwo: Mali ndi Musi. Amenewo ndiwo mabanja a Levi mwa kubadwa kwao.
20 Ndipo Amramu anadzitengera Yokobedi mlongo wa atate wace akhale mkazi wace; ndipo anambalira Aroni ndi Mose; ndi zaka za moyo wa Amramu ndizo zaria limodzi mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri.
21 Ndi ana amuna a lzara ndiwo: Kora: ndi Nefegi, ndi Zikiri.
22 Ndi ana amuna a Uziyeli ndiwo: Misayeli, ndi Elisafana, ndi Sitiri.