13 Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nafa aculewo kucokera m'zinyumba, ndi m'mabwalo, ndi m'minda.
14 Ndipo anawaola miulu-miulu; ndi dziko linanunkha.
15 Koma pamene Farao, anaona kuti panali kupuma, anaumitsa mtima wace, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.
16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Samula ndodo yako, nupande pfumbi lapansi, kuti lisanduke nsabwe m'dziko lonse la Aigupto.
17 Ndipo anacita comweco; pakuti Aroni anasamula dzanja lace ndi ndodo yace, napanda pfumbi lapansi, ndipo panali nsabwe pa anthu ndi pa zoweta; pfumbi lonse lapansi liinasanduka nsabwe m'dziko lonse la Aigupto.
18 Alembi anateronso ndi matsenga ao kuonetsa nsabwe, koma sanakhoza; ndipo panali nsabwe pa anthu, ndi pa zoweta.
19 Pamenepo alembi anati kwa Farao, Cala ca Mulungu ici; koma mtima wa Farao unalimba, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.