9 Koma Mose anati kwa Farao, Ulemu ndi wanu, wa ine ai; ndipembere inu ndi anyamata anu ndi anthu anu liti, kuti aonongeke aculewo, acokere inu ndi nyumba zanu, atsale m'nyanja mokha?
10 Ndipo anati, Mawa. Nati Mose, Kukhale monga mau anu, kuti mudziwe, kuti palibe wina wonga Yehova Mulungu wathu.
11 Ndipo acule adzacokera inu, ndi nyumba zanu, ndi anyamata anu, ndi anthu anu; adzatsala m'nyanja mokha.
12 Ndipo Mose ndi Aroni anaturuka kwa Farao; ndi Mose anapfuulira kwa Yehova kunena za acule amene adawaika pa Farao.
13 Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nafa aculewo kucokera m'zinyumba, ndi m'mabwalo, ndi m'minda.
14 Ndipo anawaola miulu-miulu; ndi dziko linanunkha.
15 Koma pamene Farao, anaona kuti panali kupuma, anaumitsa mtima wace, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.