1 Pamenepo Yehova anati kwa Mose, Lowa kwa Farao, numuuze, Atero Yehova Mulungu wa Ahebri, Lola anthu anga amuke, kuti anditumikire.
2 Pakuti ukakana kuwalola amuke, ndi kuwagwira cigwiritsire,
3 taona, dzanja la Yehova lidzakhala pa zoweta zako za kubusa, pa akavalo, pa aburu, pa ngamila, pa ng'ombe, ndi pa zoweta zazing'ono ndi kalira woopsa.
4 Ndipo Yehova adzasiyanitsa pakati pa zoweta za Israyeli ndi zoweta za Aigupto; kuti kasafe kanthu kali konse ka ana a Israyeli,