33 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Tenga mphika, nuthiremo mana odzala omeri, nuuike pamaso pa Yehova, usungikire mibadwo yanu.
34 Monga Yehova anauza Mose, momwemo Aroni anauika patsogolo pa Mboni, usungikeko.
35 Ndipo ana a Israyeli anadya mana zaka makumi anai, kufikira atalowa dziko la midzi; anadya mana kufikira analowa malire a dziko la Kanani.
36 Koma omeri ndilo limodzi la magawo khumi la efa.