1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Lankhula ndi ana a Israyeli, kuti anditengere copereka; ulandire copereka canga kwa munthu ali yense mtima wace umfunitsa mwini.
3 Ndipo coperekaco ucilandire kwa iwo ndi ici: golidi, ndi, siliva, ndi mkuwa,
4 ndi lamadzi, ndi: lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;
5 ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;