33 Ku mphanda yina kukhale zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; ndi ku mphanda inzace zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; zitere mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyalico.
34 Ndipo pa coikapo nyali comwe pakhale zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yace ndi maluwa ace;
35 pakhale mutu pansi pa mphaada ziwiri zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zoturuka m'mwemo; itere ku mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyalico.
36 Mitu yao ndi mphanda zao zikhale zoturuka m'mwemo; conseci cikhale cosulika cimodzi ca golidi woona.
37 Ndipo uzipanga nyali zace, zisanu ndi ziwiri; ndipo ayatse nyali zace, ziwale pandunji pace.
38 Ndipo mbano zace, ndi zoolera zace, zikhale za golidi woona.
39 Acipange ici ndi zipangizo izi zonse za talente wa golidi woona.