1 Ndipo Mose anayankha nati, Koma taonani, sadzakhulupirira ine, kapena kumvera mau anga; pakuti adzanena, Yehova sanakuonekera iwe.
2 Ndipo Yehova ananena naye, Ico nciani m'dzanja lako? Nati, Ndodo.
3 Ndipo ananena iye, Iponye pansi. Naiponya pansi, ndipo inasanduka njoka; ndipo Mose anaithawa.
4 Koma Yehova anati kwa Mose, Tambasula dzanja lako, nuigwire kumcira; ndipo anatambasula dzanja lace, naigwira, nikhalanso ndodo m'dzanja lace;