35 Ndipo anaomba nsaru yocinga ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; anaciomba ndi akerubi nchito ya mmisiri.
36 Ndipo anaipangira mizati inai yasitimu, nazikuta ndi golidi; zokowera zao zinali zagolidi; ndipo anaziyengera makamwa anai asiliva.
37 Ndipo anaomba nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco, ya lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula;
38 ndi nsamamira zace zisanu ndi zokowera zao; nakuta mitu yao ndi mitanda yao ndi golidi; ndi makamwa ao asanu anali amkuwa.