2 Werenga khamu lonse la ana a Israyeli, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba ya makolo ao ndi kuwerenga maina ao, amuna onse mmodzi mmodzi.
3 Iwe ndi Aroni muwawerenge monga mwa magulu ao, onse m'Israyeli akuturuka kunkhondo, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu,
4 Ndipo pamodzi ndi inu pakhale munthu mmodzi wa mapfuko onse; yense mkuru wa nyumba ya kholo lace.
5 Ndipo maina a amuna amene aime nanu ndi awa: wa Rubeni, Elizuri mwana wa Sedeuri.
6 Wa Simeoni, Selumiyeli mwana wa Zurisadai.
7 Wa Yuda, Nahesoni mwana wa Aminadabu.
8 Wa Isakara, Netaneli mwana wa Zuwara.