Numeri 27 BL92

Ana akazi a Tselofekadi

1 Pamenepo anayandikiza ana akazi a Tselofekadi mwana wa Heferi, ndiye mwana wa Gileadi, ndiye mwana wa Makiri, ndiye mwana wamwamuna wa Manase, wa mabanja a Manase mwana wa Yosefe; ndipo maina a ana ace akazi ndiwo, Mala, Nowa, Hogila ndi Milika ndi Tiriza.

2 Ndipo anaima pamaso pa Mose, ndi pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa akalonga, ndi khamu lonse, pakhomo pa cihema cokomanako, ndi kuti,

3 Atate wathu adamwalira m'cipululu, ndipo sanakhala iye pakati pa msonkhano wa iwo akusonkhana kutsutsana ndi Yehova, mu msonkhano wa Kora; koma anafera zoipa zace zace; ndipo analibe ana amuna.

4 Licotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lace, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathu lathu pakati pa abale a atate wathu.

5 Ndipo Mose anapita nao mlandu wao pamaso pa Yehova.

6 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

7 Ana akazi a Tselofekadi anena zaona; uwapatse ndithu colowa cikhale cao cao pakati pa abale a atate wao; nuwalandiritse colowa ca atate wao.

8 Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Akafa munthu wamwamuna wopanda mwana wamwamuna, colowa cace acilandire mwana wace wamkazi.

9 Ndipo akapanda kukhala naye mwana wamkazi, mupatse abale ace colowa cace.

10 Ndipo akapanda kukhala nao abale, mupatse abale a atate wace colowa cace.

11 Ndipo akapanda abale a atate wace, mupatse wa cibale cace woyandikizana naye wa pfuko lace colowa cace, likhale lace lace; ndipo likhale kwa ana a Israyeli lemba monga Yehova wamuuza Mose.

Aikidwa Yoswa mmalo mwa Mose

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kwera m'phiri ili la Abarimu, nupenye dziko limene ndapatsa ana a Israyeli,

13 Utaliona iwenso udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako, monga anaitanidwa Aroni mbale wako;

14 popeza munapikisana nao mau anga m'cipululu ca Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pa madziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba m'Kadesi, m'cipululu ca Zini.

15 Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,

16 Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, aike munthu pa khamulo,

17 wakuturuka pamaso pao, ndi kulowa pamaso pao, wakuwaturutsa ndi kuwalowetsa; kuti khamu la Ambuye lisakhale ngati nkhosa zopanda mbusa.

18 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

19 numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao.

20 Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israyeli ammvere.

21 Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa ciweruzo ca Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituruka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israyeli pamodzi naye, ndiwo khamu lonse.

22 Ndipo Mose anacita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse;

23 namuikira manja ace, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31 32 33 34 35 36