1 Pamenepo anayandikiza ana akazi a Tselofekadi mwana wa Heferi, ndiye mwana wa Gileadi, ndiye mwana wa Makiri, ndiye mwana wamwamuna wa Manase, wa mabanja a Manase mwana wa Yosefe; ndipo maina a ana ace akazi ndiwo, Mala, Nowa, Hogila ndi Milika ndi Tiriza.