Numeri 24 BL92

1 Pamene Balamu anaona kuti kudakomera pamaso pa Yehova kudalitsa Israyeli, sanamuka, monga nthawi zija zina, ku nyanga zolodzera, koma anayang'ana nkhope yace kucipululu.

2 Ndipo Balamu anakweza maso ace, naona Israyeli alikukhala monga mwa mafuko ao; ndipo mzimu wa Mulungu unadza pa iye.

3 Pamenepo ananena fanizo lace, nati,Balamu mwana wa Beori anenetsa,Ndi munthuyo anatsinzina maso anenetsa;

4 Wakumva mau a Mulungu anenetsa,Wakuona masomphenya a Wamphamvuyonse,Wakugwa pansi maso ace openyuka:

5 Ha! mahema ako ngokoma, Yakobo;Zokhalamo zako, Israyeli!

6 Ziyalika monga zigwa,Monga minda m'mphepete mwanyanja,Monga khonje waoka Yehova,Monga mikungudza m'mphepete mwa madzi.

7 Madzi adzayenda naturuka m'zotungira zace,Ndi mbeu zace zidzakhala ku madzi ambiri,Ndi mfumu yace idzamveka koposa Agagi,Ndi ufumu wace udzamveketsa.

8 Mulungu amturutsa m'Aigupto;Ali nayo mphamvu yonga ya njati;Adzawadya amitundu, ndiwo adani ace.Nadzaphwanya mafupa ao, Ndi kuwapyoza ndi mibvi yace.

9 Anaunthama, nagona pansi ngati mkango,Ngati mkango waukazi; adzamuutsa ndani?Wodalitsika ali yense wakudalitsa iwe,Wotemberereka ali yense wakutemberera iwe.

10 Pamenepo Balaki anapsa mtima pa Balamu, naomba m'manja; ndipo Balaki anati kwa Balamu, Ndinakuitana kutemberera adani ansa, ndipo unawadalitsa ndithu katatu tsopano.

11 Cifukwa cace thawira ku malo ako tsopano; ndikadakucitira ulemu waukuru; koma, taona, Yehova wakuletsera ulemu.

12 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Kodi sindinauzanso amithenga anu amene munawatumiza kwa ine, ndi kuti,

13 Cinkana Balaki akandipatsa nyumba yace yodzala ndi siliva ndi golidi, sindikhoza kutumpha mau a Yehova, kucita cokoma kapena coipa ine mwini wace; conena Yehova ndico ndidzanena ine?

14 Ndipo tsopano, taonani, ndimuka kwa anthu a mtundu wanga; tiyeni, ndidzakulangizani, ndi kukuuzani zimene anthu awa adzacitira anthu anu, masiku otsiriza.

15 Ndipo ananena fanizo lace, nati,Balamu mwana wa Beori anenetsa,Ndi munthu wotsinzina masoyo anenetsa;

16 Anenetsa wakumva mau a Mulungu,Ndi kudziwa nzeru ya Wam'mwambamwamba,Wakuona masomphenya a Wamphamvuyonse,Wakugwa pansi wopenyuka maso;

17 Ndimuona, koma tsopano ai; Ndimpenya, koma si pafupi ai;Idzaturuka nyenyezi m'Yakobo,Ndi ndodo yacifumu idzauka m'Israyeli,Nidzakantha malire a Moabu,Nidzapasula ana onse a Seti,

18 Ndi Edomu adzakhala ace ace,Seiri lomwe lidzakhala lace lace, ndiwo adani ace;

19 Koma Israyeli adzacita zamphamvu.Ndipo wina woturuka m'Yakobo adzacita ufumu;Nadzapasula otsalira m'mudzi.

20 Ndipo anayang'ana ku Amaleki, nanena fanizo lace, nati,Amaleki ndiye woyamba wa amitundu;Koma citsiriziro cace, adzaonongeka ku nthawi zonse.

21 Ndipo anayang'ana Akeni, nanena fanizo lace, nati,Kwanu nkokhazikika,Wamanga cisa cako m'thanthwe.

22 Koma Kaini adzaonongeka,Kufikira Asuri adzakumanga nsinga.

23 Ndipo ananena fanizo lace, nati,Ha! adzakhala ndi moyo ndani pakucita ici Mulungu?

24 Koma zombo zidzafika kucokera ku doko la Kitimu,Ndipo adzasautsa Asuri, nadzasautsa Ebere,Koma iyenso adzaonongeka.

25 Ndipo Balamu anauka, namuka nabwerera kumalo kwace; ndi Balaki yemwe anamka njira yace.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31 32 33 34 35 36