4 Ndipo pamodzi ndi inu pakhale munthu mmodzi wa mapfuko onse; yense mkuru wa nyumba ya kholo lace.
5 Ndipo maina a amuna amene aime nanu ndi awa: wa Rubeni, Elizuri mwana wa Sedeuri.
6 Wa Simeoni, Selumiyeli mwana wa Zurisadai.
7 Wa Yuda, Nahesoni mwana wa Aminadabu.
8 Wa Isakara, Netaneli mwana wa Zuwara.
9 Wa Zebuloni, Eliyabu mwana wa Heloni.
10 Wa ana a Yosefe: wa Efraimu, Elisama mwana wa Amihudi; wa Manase, Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.