2 Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.
3 Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,
4 Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.
5 Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.
6 Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.
7 Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.
8 Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.