23 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Manase anayang'anira Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.
24 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Benjamini anayang'anira Abidana mwana wa Gideoni.
25 Pamenepo anayenda a mbendera ya cigono ca ana a Dani, ndiwo a m'mbuyombuyo a zigono zonse, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lace anayang'anira Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Aseri anayang'anira Pagiyeli mwana wa Okirani.
27 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Nafitali anayang'anira Ahira mwana wa Enani.
28 Potero maulendo a ana a Israyeli anakhala monga mwa magulu ao; nayenda ulendowao.
29 Ndipo Mose anati kwa Hobabu mwana wa Reueli Mmidyani mpongozi wa Mose, Ife tirikuyenda kumka ku malo amene Yehova anati, Ndidzakupatsani awa; umuke nafe, tidzakucitira zokoma; popeza Yehova wanenera Israyeli zokoma.