17 Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uwu pali madyerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda cotupitsa.
18 Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena;
19 koma mubwere nayo nsembe yamoto, nsembe yopsereza ya Yehova; ng'ombe ziwiri zamphongo, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi; akhale kwa inu opanda cirema;
20 ndi nsembe yao ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta; mupereke atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe, ndi awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo;
21 upereke limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi; uzitero ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;
22 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo, yakutetezera inu.
23 Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza ya m'mawa, ndiyo ya nsembe yopsereza kosalekeza.