19 Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amiramu ndi lzara, Hebroni ndi Uziyeli.
20 Ndi ana a Merari monga mwa mabanja ao: Mali ndi Musi. Awa ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.
21 Banja la Libini, ndi mabanja a Simei, ndiwo a Gerisoni; ndiwo mabanja a Gerisoni.
22 Owerengedwa ao, powawerenga amuna onse, kuyambira mwana wa mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.
23 Mabanja a Agerisoni azimanga mahema ao pambuyo pa kacisi kumadzulo.
24 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo a Agerisoni ndiye Eliyasafe mwana wa Layeli.
25 Ndipo udikiro wa ana a Gerisoni m'cihema cokomanako ndiwo kacisi, ndi cihema, cophimba cace, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihema cokomanako,