27 Banja la Aamiramu, ndi banja la Aizara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyeli ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.
28 Powawerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi, akusunga udikiro wa pa malo opatulika.
29 Mabanja a ana a Kohati azimanga mahema ao pa mbali ya kacisi ya kumwera.
30 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo ao ya mabanja a Akohati ndiye Elizafana mwana wa Uziyeli.
31 Ndipoudikirowaondiwo likasa, ndi gome, ndi coikapo nyali, ndimagome a nsembe, ndi zipangizo za malo opatulika zimene acita nazo, ndi nsaru yocinga, ndi nchito zace zonse.
32 Ndipo kalonga wa akalonga a Alevi ndiye Eleazara mwana wa Aroni wansembeyo; ndiye aziyang'anira osunga udikiro wa pa malo opatulika.
33 Banja la Amali, ndi banja la Amusi ndiwo a Merari; ndiwo mabanja a Merari.