4 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamaso pa Yehova muja anabwera nao moto wacilendo pamaso pa Yehova, m'cipululu ca Sinai, ndipo analibe ana; koma Eleazara ndi Itamara anacita Debito ya nsembe pamaso pa atate wao Aroni.
5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
6 Sendera nalo kuno pfuko la Levi, ndi kuwaika pamaso pa Aroni wansembe, kuti amtumikire.
7 Ndipo azisunga udikiro wace, ndi udikiro wa khamu lonse pa khomo la cihema cokomanako, kucita nchito ya kacisi.
8 Ndipo asunge zipangizo zonse za cihema cokomanako, ndi udikiro wa ana a Israyeli, kuicita nchito ya kacisi.
9 Ndipo uzipereka Alevi kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna; apatsidwa kwa iye ndithu, ocokera kwa ana a Israyeli.
10 Koma uike Aroni ndi ana ace amuna, azisunga nchito yao ya nsembe; ndi mlendo wakusendera pafupi amuphe.