34 Ndipo ana a Gadi anamanga Diboni, ndi Ataroti, ndi Aroeri;
35 Ataroti Sofani, Yazeri, ndi Yogebeha;
36 ndi Beti Nimira, ndi Beti Harani: midzi ya m'malinga, ndi makola a zoweta.
37 Ndipo ana a Rubeni anamanga Hesiboni, ndi Eleyali, ndi Kiriyataimu;
38 ndi Nebo, ndi Baala Meoni (nasintha maina ao), ndi Sibima; ndipo anaicha midzi adaimanga ndi maina ena.
39 Ndipo ana a Makiri mwana wa Manase anamka ku Gileadi, naulanda, napitikitsa Aamori anali m'mwemo.
40 Ndipo Mose anapatsa Makiri mwana wa Manase Gileadi; ndipo anakhala m'menemo.