4 pamene Aaigupto ailalikuika oyamba kubadwa ao onse, amene Yehova adawakantha; Yehova adaweruzanso milungu yao.
5 Ndipo ana a Israyeli macokera ku Ramese, nayenda namanga ku Sukoti.
6 Nacokera ku Sukoti, nayenda namanga m'Etamu, ndiko ku malekezero a cipululu.
7 Ndipo anacokera ku Etamu, nayenda nabwerera ku Pihahiroti, ndiko kutsogolo kwace kwa Baala Zefoni; namanga iwo patsogolo pa Migidoli.
8 Ndipo anacokera ku Pihahiroti, naoloka pakati pa nyanja nalowa m'cipululu; nayenda ulendo wa masiku atatu m'cipululu ca Etamu, namanga m'Mara.
9 Ndipo anacokera ku Mara, nayenda nafika ku Elimu, ku Elimu ndiko kuli akasupe khumi ndi awiri a madzi, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; namanga iwo komweko.
10 Ndipo anacokera ku Elimu, nayenda namanga ku Nyanja Yofiira.