18 Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.
19 Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.
20 Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.
21 Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.
22 Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.
23 Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.
24 Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.