9 Ndipo ubwere nao Alevi pakhomo pa cihema cokomanako; nuwasonkhanitse khamu lonse la ana a Israyeli;
10 nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israyeli aike manja ao pa Alevi;
11 ndi Aroni apereke Alevi ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, yocokera kwa ana a Israyeli, kuti akhale akucita nchito ya Yehova,
12 Ndipo Alevi aike manja ao pa mitu ya ng'ombezo; pamenepo ukonze imodzi ikhale nsembe yaucimo, ndi inzace, nsembe yopsereza za Yehova, kucita cotetezera Alevi.
13 Ndipo uimike Alevi pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ace, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
14 Momwemo upatule Alevi mwa ana a Israyeli; kuti Alevi akhale anga.
15 Ndipo atatero alowe Alevi kucita Debito ya cihema cokomanako; ndipo uwayeretse, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula.