1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, mwezi woyamba wa caka caciwiri ataturuka m'dziko la Aigupto, ndi kuti,
2 Ana a Israyeli acite Paskha pa nyengo yoikidwa.
3 Tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, muziucita, pa nyengo yace yoikidwa; muucite monga mwa malemba ace onse, ndi maweruzo ace onse.
4 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, kuti acite Paskha.