7 nanena naye amunawa, Tadetsedwa ife ndi mtembo wa munthu; atiletseranji, kuti tisabwere naco copereka ca Yehova pa nyengo yace yoikidwa, pakati pa ana a Israyeli?
8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve couza Yehova za inu.
9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
10 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, cifukwa ca mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azicitira Yehova Paskha.
11 Mwezi waciwiri, tsiku lace lakhumi ndi cinai, madzulo, aucite; audye ndi mkate wopanda cotupitsa ndi msuzi wowawa.
12 Asasiyeko kufikira m'mawa, kapena kuthyolapo pfupa; aucite monga mwa lemba lonse la Paskha.
13 Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kucita Paskha, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wace; popeza sanabwera naco copereka ca Yehova pa nyengo yace yoikidwa, munthuyu asenze kucimwa kwace.