1 Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, napfuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.
2 Ndipo ana onse a Israyeli anadandaulira Mose ndi Aroni; ndi khamu lonse linanena nao, Mwenzi tikadafa m'dziko la Aigupto; kapena mwenzi tikadafa m'cipululu muno!
3 Ndipo Yehova atitengeranii kudza nafe kudziko kuno, kuti tigwe nalo lupanga? Akazi athu ndi makanda athu adzakhala cakudya cao; kodi sikuli bwino tibwerere ku Aigupto?
4 Ndipo anati wina ndi mnzace, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Aigupto.
5 Pamenepo Mose ndi Aroni anagwa nkhope pansi pamaso pa msonkhano wonse wa khamu la ana a Israyeli.
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, ndiwo a iwo aja adazonda dzikolo, anang'amba zobvala zao;