16 Pakhale cilamulo cimodzi ndi ciweruzo cimodzi kwa inu ndi kwa mlendo wakukhala kwanu.
17 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
18 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene mulowa m'dziko limene ndirikukulowetsani,
19 kudzali, pakudya inu mkate wa m'dzikolo, muzikwezera Yehova nsembe yokweza.
20 Pa mtanda wanu woyamba muperekeko kamtanda, kakhale nsembe yokweza; monga mumacitira nsembe yokweza ya popuntha tirigu, momwemo muzikakweza.
21 Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.
22 Ndipo pamene mulakwa, osacita mau awa onse amene Yehova ananena ndi Mose;