10 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kulika cakuno ca mboni, isungike ikhale cizindikilo ca pa ana opikisana; kuti unelitsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.
11 Ndipo Mose anacita monga Yehova adamuuza, momwemo anacita.
12 Pamenepo ana a Israyeli ananena ndi Mose, nati, Taonani, tikufa, tionongeka, tionongeka tonse.
13 Yense wakuyandikiza kacisi wa Yehova amwalira; kodi tidzatha nkufa?