24 Yasubi, ndiye kholo la banja la Ayasubi; Simironi, ndiye kholo la banja la Asimironi.
25 Iwo ndiwo mabanja a Isakara monga mwa owerengedwa ao; zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana atatu.
26 Ana amuna a Zebuloni monga mwa mabanja ao ndiwo: Seredi, ndiye kholo la banja la Aseredi; Eloni, ndiye kholo la banja la Aeloni; Yahaliyeli, ndiye kholo la banja la Ayahaliyeli.
27 Iwo ndiwo mabanja a Zebuloni monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu mazana asanu.
28 Ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao ndiwo: Manase ndi Efraimu.
29 Ana a Manase ndiwo: Makiri, ndiye kholo la banja la Amakiri; ndipo Makiri anabala Gileadi; ndiye kholo la banja la Agileadi,
30 Ana a Gileadi ndiwo: Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Heleki, ndiye kholo la banja la Aheleki;