13 Pakuti ana oyamba onse ndi anga; tsiku lija ndinakantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto ndinadzipatulira ana oyamba onse m'Israyeli, kuyambira munthu kufikira coweta; ndiwo anga; Ine ndine Yehova.
14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, nati,
15 Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.
16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.
17 Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Gerisoni, ndi Kohati ndi Merari.
18 Ndi ana a Gerisoni maina ao ndi awa, monga mwa mabanja ao: Libini, ndi Simei.
19 Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amiramu ndi lzara, Hebroni ndi Uziyeli.