44 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
45 Landira Alevi m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli, ndi ng'ombe za Alevi m'malo mwa ng'ombe zao; ndipo Alevi azikhala anga; Ine ndine Yehova.
46 Kunena za mazana awiri ndi makumi asanu ndi awiri kudza atatuwo oyamba kubadwa a ana a Israyeli, akuposa Alevi, akaomboledwe,
47 ulandire masekeli asanu pa munthu mmodzi; uwalandire pa muyeso wa sekeli wa malo opatulika (sekeli ndiwo magera makumi awiri);
48 nupereke ndarama zimene akuposawo anaomboledwa nazo kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna.
49 Pamenepo Mose analandira ndarama zaom bola nazo kwa iwo akuposa aja adawaombola Alevi;
50 analandira ndaramazo kwa oyamba kubadwa a ana a Israyeli; masekeli cikwi cimodzi mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu, kuyesa sekeli wa malo opatulika.