4 ndipo atate wace akamva cowinda cace, ndi codziletsa cace anamanga moyo wace naco, koma wakhala naye cete atate wace; pamenepo zowinda zace zonse zidzakhazikika, ndi codziletsa ciri: conse wamanga naco moyo wace cidzakhazikika.
5 Koma atate wace akamletsa tsiku lakumva iye; zowinda zace zonse, ndi zodziletsa zace zonse anamanga nazo moyo wace, sizidzakhazikika; ndipo Yehova adzamkhululukira, popeza atate wace anamletsa.
6 Ndipo akakwatibwa naye mwamuna, pokhala ali nazo zowinda zace, kapena zonena zopanda pace za milomo yace, zimene anamanga nazo moyo wace;
7 nakazimva mwamuna wace, nakakhala naye cete tsiku lakuzimva iye; pamenepo zowinda zace zidzakhazikika, ndi zodziletsa anamanga nazo moyo wace zidzakhazikika.
8 Kama mwamuna wace akamletsa tsiku lakumva iye; pamenepo adzafafaniza cowinda cace anali naco, ndi zonena zopanda pace za milomo yace, zimene anamanga nazo moyo wace; ndipo Yehova adzamkhululukira.
9 Koma cowinda ca mkazi wamasiye, kapena mkazi wocotsedwa, ziti zonse anamanga nazo moyo wace zidzamkhazikikira.
10 Ndipo ngati anawinda m'nyumba ya mwamuna wace, kapena anamanga moyo wace ndi codziletsa ndi kulumbirapo,