22 ndi dziko lagonjera Yehova; mutatero mudzabwerere, ndi kukhala osacimwira Yehova ndi Israyeli; ndipo dziko ili lidzakhala lanu lanu pamaso pa Yehova.
23 Koma mukapanda kutero, taonani, mwacimwira Yehova; ndipo zindikirani kuti cimo lanu lidzakupezani.
24 Dzimangireni midzi ya ana anu, ndi makola a zoweta zanu; ndipo muzicite zoturuka m'kamwa mwanu.
25 Ndipo ana a Gadi ndi ana a Rubeni ananena ndi Mose, nati, Anyamata anu adzacita monga mbuyanga alamulira.
26 Ana athu, akazi athu, zoweta zathu, ndi ng'ombe zathu zonse, zidzakhala komweko m'midzi ya ku Gileadi;
27 koma anyamata anu adzaoloka, yense wokonzekera ndi zankhondo pamaso pa Yehova kunkhondo, monga wanena mbuyanga.
28 Pamenepo Mose anamuuza Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akuru a makolo a mapfuko a ana a Israyeli za iwo.