31 Musamalandira dipo lakuombola moyo wa iye adapha munthu, naparamula imfa; koma aziphedwa ndithu.
32 Musamalandira dipo lakuombola iye amene adathawira ku mudzi wace wopulumukirako, kuti abwerenso kukhala m'dziko, kufikira atafa wansembe.
33 Ndipo musamaipsa dziko muli m'mwemo; popeza mwazi uipsa dziko; pakuti kulibe kutetezera dziko cifukwa ca mwazi anaukhetsa m'mwemo, koma ndi mwazi wa iye anaukhetsa ndiwo.
34 Usamadetsa dziko ukhala m'mwemo, limene ndikhalitsa pakati pace; popeza Ine Yehova ndikhalitsa pakati pa ana a Israyeli.