3 Ndipo akakwatibwa nao ana amuna a mapfuko ena a ana a Israyeli, acicotse colowa cao ku colowa ca makolo athu, nacionjeze ku colowa ca pfuko limene adzakhalako; cotero acicotse ku maere a colowa cathu.
4 Ndipo pofika caka coliza ca ana a Israyeli adzaphatikiza colowa cao ku colowa ca pfuko limene akhalako; cotero adzacotsa colowa cao ku colowa ca pfuko la makolo athu.
5 Ndipo Mose analamulira ana a Israyeli monga mwa mau a Yehova, nati, Pfuko la ana a Yosefe linena zaona.
6 Colamulira Yehova za ana akazi a Tselofekadi ndi ici, kuti, Akwatibwe nao amene afuna eni ace; komatu akwatibwe nao a banja la pfuko la makolo ao okha okha.
7 Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko; popeza ana a Israyeli adzamamatira yense ku colowa ca pfuko la makolo ace.
8 Ndipo mwana wamkazi yense wa mapfuko a ana a Israyeli, wakukhala naco colowa, akwatibwe ndi wina wa banja la pfuko la kholo lace, kuti ana a Israyeli akhale naco yense colowa ca makolo ace.
9 Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko, pakuti mapfuko a ana a Israyeli adzamamatira lonse ku colowa cace cace.