6 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwamuna kapena mkazi akacita cimo liri lonse amacita anthu, kucita mosakhulupirika pa Yehova, nakaparamuladi;
7 azibvomereza cimo lace adalicita; nabwezere coparamulaco monsemo, naonjezeko limodzi la magawo asanu, ndi kucipereka kwa iye adamparamulayo.
8 Koma munthuyo akapanda kukhala nayo nkhoswe imene akaibwezere coparamulaco, coparamula acibwezera Yehovaco cikhale ca wansembe; pamodzi ndi nkhosa yamphongo ya cotetezerapo, imene amcitire nayo comtetezera.
9 Ndipo nsembe zokweza zonse za zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zimene abwera nazo kwa wansembe zisanduka zace.
10 Zopatulika za munthu ali yense ndi zace: ziti zonse munthu ali yense akapatsa wansembe, zasanduka zace.
11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
12 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mkazi wa mwini akapatukira mwamuna wace, nakamcitira mosakhulupirika,